| 🏆Uthenga Wabwino kwa anthu a m’Buku (Akhrisitu ndi Ayuda) amene adalowa Chisilamu 👇🏾
Mtumiki Muhammad mtendere ndi madalitso zikhale pa iye anati: |
---|
🌿"Anthu amitundu itatu adzalandira malipiro awiri: |
🌿"M'modzi mwa anthu a m'Buku (Mkhristu kapena Myuda) amene amakhulupirira 👉🏽 Mneneri wake ndi kukhulupilira Muhammad". |
Mulungu Wamphamvuzonse, Allah , amapereka mphoto kwa amene sali Msilamu, ngati alandira Chisilamu, pa zabwino zonse zomwe adazichita asanakhale Msilamu, ngati sizikutsutsana ndi chiphunzitso cha Chisilamu monga: |
✔️Kupereka zachifundo ndi ✔️kulemekeza makolo. |
Ichi ndi chimodzi mwachisomo chachikulu cha Mulungu wapamwambamwamba (Allah) ndipo chimalimbikitsa osakhulupirira kuti alowe Chisilamu. |
🌿 Hakim bin Hizam adati kwa Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye): |
| 🌿"Ndisanalowe m'Chisilamu ndidali kuchita zabwino monga kupereka sadaka, kumasula akapolo ndi kukhala ndi ubale wabwino ndi makolo ndi achibale. Kodi ndidzalipidwa pazimenezo?" Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) anayankha kuti:
"Udakhala Asilamu ndi zabwino zonsezo (Posataya malipiro awo).” |
---|