| 🏆Uthenga Wabwino kwa anthu a m’Buku (Akhrisitu ndi Ayuda) amene adalowa Chisilamu 👇🏾

Mtumiki Muhammad mtendere ndi madalitso zikhale pa iye anati:
🌿"Anthu amitundu itatu adzalandira malipiro awiri:
🌿"M'modzi mwa anthu a m'Buku (Mkhristu kapena Myuda) amene amakhulupirira 👉🏽 Mneneri wake ndi kukhulupilira Muhammad".
Mulungu Wamphamvuzonse, Allah , amapereka mphoto kwa amene sali Msilamu, ngati alandira Chisilamu, pa zabwino zonse zomwe adazichita asanakhale Msilamu, ngati sizikutsutsana ndi chiphunzitso cha Chisilamu monga:
✔️Kupereka zachifundo ndi ✔️kulemekeza makolo.
Ichi ndi chimodzi mwachisomo chachikulu cha Mulungu wapamwambamwamba (Allah) ndipo chimalimbikitsa osakhulupirira kuti alowe Chisilamu.
🌿 Hakim bin Hizam adati kwa Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye):

| 🌿"Ndisanalowe m'Chisilamu ndidali kuchita zabwino monga kupereka sadaka, kumasula akapolo ndi kukhala ndi ubale wabwino ndi makolo ndi achibale. Kodi ndidzalipidwa pazimenezo?" Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) anayankha kuti:

"Udakhala Asilamu ndi zabwino zonsezo (Posataya malipiro awo).”