| Ndikuganiza kuti kukhala pakati pa Akhristu kumakhudza kwambiri chikhulupiriro chanu mwa Allah . Muyenera kukonza chikhulupiriro chanu kapena simungathe kulowa paradiso. Mulungu alibe ana palibe banja,
| Allah sabala. |
|---|
| 📍Umboni wotani woti Allah alibe mwana? |
| Allah akunena mu Qur'an (kumasulira tanthauzo) chaputala (112): |
| Nena (iwe Mtumiki (s.a.w), kwa amene akukufunsa mwachipongwe, mbiri za Mulungu wako): “Iye ndi Allah Mmodzi, (alibe mnzake). |
| Allah ndi Wokhala ndi zonse Wodaliridwa ndi zolengedwa Zake. |
| Sadabale (mwana) ndiponso sadaberekedwe. |
| Ndiponso palibe aliyense wofanana ndi Iye.” |
| (Quran:112) |
| Mumakhulupirira Qur'an, ndipo mukuyenera kukhulupilira kuti Allah alibe mwana monga m'Qur'an yanenera. |
| Komanso Allah ndi Wokwanira |
| Iye alibe chifukwa choti ana akhale ndi moyo pambuyo pake. |
| Iye safuna ana kuti amuthandize. |
| Zolengedwa zonse zimafuna Mulungu, ndipo Mulungu safuna aliyense. |